8. Anakwera m'mapiri, anatsikira m'zigwa,Kufikira malo mudawakonzeratu.
9. Munaika malire kuti asapitirireko;Kuti asabwererenso kuphimba dziko lapansi.
10. Atumiza akasupe alowe m'makwawa;Ayenda pakati pa mapiri:
11. Zimamwamo nyama zonse za kuthengo;Mbidzi zipherako ludzu lao.
12. Mbalame za mlengalenga zifatsa pamenepo,Zimayimba pakati pa mitawi.
13. Iye amwetsa mapiri mocokera m'zipinda zace:Dziko lakhuta zipatso za nchito zanu.
14. Ameretsa msipu ziudye ng'ombe,Ndi zitsamba acite nazo munthu;Naturutse cakudya cocokera m'nthaka;
15. Ndi vinyo wokondweretsa mtima wa munthu,Ndi mafuta akunyezimiritsa nkhope yace,Ndi mkate wakulimbitsa mtima wa munthu.
16. Mitengo ya Mulungu yadzala ndi madzi;Mikungudza ya ku Lebano imene anaioka;
17. M'mwemo mbalame zimanga zisa zao;Pokhala cumba mpa mitengo ya mikungudza,
18. Mapiri atali ndiwo ayenera zinkhoma;Pamatanthwe mpothawirapo mbira.