Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 104:7-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Pa kudzudzula kwanu anathawa;Anathawa msanga liu la bingu lanu;

8. Anakwera m'mapiri, anatsikira m'zigwa,Kufikira malo mudawakonzeratu.

9. Munaika malire kuti asapitirireko;Kuti asabwererenso kuphimba dziko lapansi.

10. Atumiza akasupe alowe m'makwawa;Ayenda pakati pa mapiri:

11. Zimamwamo nyama zonse za kuthengo;Mbidzi zipherako ludzu lao.

12. Mbalame za mlengalenga zifatsa pamenepo,Zimayimba pakati pa mitawi.

13. Iye amwetsa mapiri mocokera m'zipinda zace:Dziko lakhuta zipatso za nchito zanu.

14. Ameretsa msipu ziudye ng'ombe,Ndi zitsamba acite nazo munthu;Naturutse cakudya cocokera m'nthaka;

15. Ndi vinyo wokondweretsa mtima wa munthu,Ndi mafuta akunyezimiritsa nkhope yace,Ndi mkate wakulimbitsa mtima wa munthu.

16. Mitengo ya Mulungu yadzala ndi madzi;Mikungudza ya ku Lebano imene anaioka;

17. M'mwemo mbalame zimanga zisa zao;Pokhala cumba mpa mitengo ya mikungudza,

18. Mapiri atali ndiwo ayenera zinkhoma;Pamatanthwe mpothawirapo mbira.

19. Anaika mwezi nyengo zace;Dzuwa lidziwa polowera pace.

20. Muika mdima ndipo pali usiku;Pamenepo zituruka zirombo zonse za m'thengo.

21. Misona ya mkango ibangula potsata nyama yao,Nifuna cakudya cao kwa Mulungu.

22. Poturuka dzuwa, zithawa, Zigona pansi m'ngaka mwao.

23. Pamenepo munthu aturukira ku nchito yace,Nagwiritsa kufikira madzulo.

24. Nchito zanu zicurukadi, Yehova!Munazicita zonse mwanzeru;Dziko lapansi lidzala naco cuma canu.

25. Nyanja siyo, yaikuru ndi yacitando,M'mwemo muli zokwawa zosawerengeka;Zamoyo zazing'ono ndi zazikuru.

26. M'mwemo muyenda zombo;Ndi livyatanu amene munamlenga aseweremo.

27. Izi zonse zikulindirirani,Muzipatse cakudya cao pa nyengo yace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 104