6. Mudalikuta ndi nyanja ngati ndi cobvala;Madzi anafikira pamwamba pa mapiri,
7. Pa kudzudzula kwanu anathawa;Anathawa msanga liu la bingu lanu;
8. Anakwera m'mapiri, anatsikira m'zigwa,Kufikira malo mudawakonzeratu.
9. Munaika malire kuti asapitirireko;Kuti asabwererenso kuphimba dziko lapansi.
10. Atumiza akasupe alowe m'makwawa;Ayenda pakati pa mapiri: