Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 104:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Anakhazika dziko lapansi pa maziko ace,Silidzagwedezeka ku nthawi yonse.

6. Mudalikuta ndi nyanja ngati ndi cobvala;Madzi anafikira pamwamba pa mapiri,

7. Pa kudzudzula kwanu anathawa;Anathawa msanga liu la bingu lanu;

8. Anakwera m'mapiri, anatsikira m'zigwa,Kufikira malo mudawakonzeratu.

9. Munaika malire kuti asapitirireko;Kuti asabwererenso kuphimba dziko lapansi.

10. Atumiza akasupe alowe m'makwawa;Ayenda pakati pa mapiri:

Werengani mutu wathunthu Masalmo 104