Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 104:19-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Anaika mwezi nyengo zace;Dzuwa lidziwa polowera pace.

20. Muika mdima ndipo pali usiku;Pamenepo zituruka zirombo zonse za m'thengo.

21. Misona ya mkango ibangula potsata nyama yao,Nifuna cakudya cao kwa Mulungu.

22. Poturuka dzuwa, zithawa, Zigona pansi m'ngaka mwao.

23. Pamenepo munthu aturukira ku nchito yace,Nagwiritsa kufikira madzulo.

24. Nchito zanu zicurukadi, Yehova!Munazicita zonse mwanzeru;Dziko lapansi lidzala naco cuma canu.

25. Nyanja siyo, yaikuru ndi yacitando,M'mwemo muli zokwawa zosawerengeka;Zamoyo zazing'ono ndi zazikuru.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 104