Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 104:1-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Lemekeza Yehova, moyo wanga;Yehova, Mulungu wanga, Inu ndinu wamkurukuru;

2. Mubvala ulemu ndi cifumu.Amene mudzikuta nako kuunika monga ndi cobvala;Ndi kuyala thambo ngati nsaru yocinga;

3. Amene alumikiza mitanda ya zipinda zace m'madzi;Naika makongwa akhale agareta ace;Nayenda pa mapiko a mphepo;

4. Amene ayesa mphepo amithenga ace;Lawi la moto atumiki ace;

5. Anakhazika dziko lapansi pa maziko ace,Silidzagwedezeka ku nthawi yonse.

6. Mudalikuta ndi nyanja ngati ndi cobvala;Madzi anafikira pamwamba pa mapiri,

7. Pa kudzudzula kwanu anathawa;Anathawa msanga liu la bingu lanu;

8. Anakwera m'mapiri, anatsikira m'zigwa,Kufikira malo mudawakonzeratu.

9. Munaika malire kuti asapitirireko;Kuti asabwererenso kuphimba dziko lapansi.

10. Atumiza akasupe alowe m'makwawa;Ayenda pakati pa mapiri:

11. Zimamwamo nyama zonse za kuthengo;Mbidzi zipherako ludzu lao.

12. Mbalame za mlengalenga zifatsa pamenepo,Zimayimba pakati pa mitawi.

13. Iye amwetsa mapiri mocokera m'zipinda zace:Dziko lakhuta zipatso za nchito zanu.

14. Ameretsa msipu ziudye ng'ombe,Ndi zitsamba acite nazo munthu;Naturutse cakudya cocokera m'nthaka;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 104