Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 5:12-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Anawapacika akalonga manja ao;Sanalemekeza nkhope za akulu.

13. Anyamata ananyamula mphero,Ana nakhumudwa posenza nkhuni.

14. Akulu adatha kuzipata,Anyamata naleka nyimbo zao.

15. Cimwemwe ca mtima wathu calekeka,Masewera athu asanduka maliro.

16. Korona wagwa pamutu pathu;Kalanga ife! pakuti tinacimwa.

17. Cifukwa ca ici mtima wathu ufoka,Cifukwa ca izi maso athu acita cimbuuzi;

18. Pa phiri la Ziyoni lopasukaloAnkhandwe ayendapo.

19. Inu, Yehova, mukhala cikhalire,Ndi mpando wanu wacifumu ku mibadwo mibadwo.

20. Bwanji mutiiwala ciiwalire,Ndi kutisiya masiku ambirimbiri;

21. Mutitembenuzire kwa Inu, Yehova, ndipo tidzatembenuzidwadi,Mukonzenso masiku athu ngati kale lija.

22. Koma mwatikaniza konse,Mwatikwiyira kopambana.

Werengani mutu wathunthu Maliro 5