Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 5:11-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Anaipitsa akazi m'Ziyoni,Ndi anamwali m'midzi ya Yuda.

12. Anawapacika akalonga manja ao;Sanalemekeza nkhope za akulu.

13. Anyamata ananyamula mphero,Ana nakhumudwa posenza nkhuni.

14. Akulu adatha kuzipata,Anyamata naleka nyimbo zao.

15. Cimwemwe ca mtima wathu calekeka,Masewera athu asanduka maliro.

16. Korona wagwa pamutu pathu;Kalanga ife! pakuti tinacimwa.

17. Cifukwa ca ici mtima wathu ufoka,Cifukwa ca izi maso athu acita cimbuuzi;

18. Pa phiri la Ziyoni lopasukaloAnkhandwe ayendapo.

19. Inu, Yehova, mukhala cikhalire,Ndi mpando wanu wacifumu ku mibadwo mibadwo.

20. Bwanji mutiiwala ciiwalire,Ndi kutisiya masiku ambirimbiri;

Werengani mutu wathunthu Maliro 5