8. Maonekedwe ao ada koposa makala, sazindikirika m'makwalala;Khungu lao limamatira pa mafupa ao, lakhwinyata, lasanduka ngati ndodo.
9. Ophedwa ndi lupanga amva bwino kupambana ophedwa ndi njala;Pakuti amenewa angokwalika napyozedwa, posowa zipatso za m'munda.
10. Manja a akazi acisoni anaphika anaanao;Anali cakudya cao poonongeka mwana wamkazi wa anthu a mtundu wanga.
11. Yehova wakwaniritsa kuzaza kwace, watsanulira ukali wace;Anayatsa moto m'Ziyoni, unanyambita maziko ace,
12. Mafumu a dziko lapansi sanakhulupirira, ngakhale onse okhala kunja kuno,Kuti adani ndi amaliwongo adzalowadi m'zipata za Yerusalemu.
13. Ndico cifukwa ca macimo a aneneri ndi mphulupulu za ansembeace,Amene anakhetsa mwazi wa olungama pakati pace.