Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Tsoka a anthu Avuda

1. Ha! golidi wagugadi; golidi woona woposa wasandulika;Miyala ya malo opatulika yakhutulidwa pa malekezero a makwalalaonse.

2. Ana a Ziyoni a mtengo wapatari, olingana ndi golidi woyengetsa,Angoyesedwa ngati mbiya zadothi zozipanga manja a woumba.

3. Angakhale ankhandwe amapatsa bere, nayamwitsa ana ao;Koma mwana wamkazi wa anthu amtundu wanga wasanduka wankhanza, ngati nthiwatiwa za m'cipululu.

4. Lilime la mwana woyamwa limamatira kumalakalaka kwace ndi ludzu;Ana ang'ono apempha mkate koma palibe wakuwanyemera.

5. Omwe anadya zolongosoka angosiyidwa m'makwalala;Omwe analeredwa nabvekedwa mlangali afungatira madzala.

6. Pakuti mphulupulu ya mwana wamkazi wa anthu amtundu wanga, ikula koposa cimo la Sodomu,Umene unapasuka m'kamphindi, anthu osaucitira kanthu.

7. Omveka ace anakonzeka koposa cipale cofewa, nayera koposa mkaka,Matupi ao anafiira koposa timiyala toti pyu; maonekedwe ao ananga a safiro wa mtengo wapatari.

8. Maonekedwe ao ada koposa makala, sazindikirika m'makwalala;Khungu lao limamatira pa mafupa ao, lakhwinyata, lasanduka ngati ndodo.

9. Ophedwa ndi lupanga amva bwino kupambana ophedwa ndi njala;Pakuti amenewa angokwalika napyozedwa, posowa zipatso za m'munda.

10. Manja a akazi acisoni anaphika anaanao;Anali cakudya cao poonongeka mwana wamkazi wa anthu a mtundu wanga.

11. Yehova wakwaniritsa kuzaza kwace, watsanulira ukali wace;Anayatsa moto m'Ziyoni, unanyambita maziko ace,

12. Mafumu a dziko lapansi sanakhulupirira, ngakhale onse okhala kunja kuno,Kuti adani ndi amaliwongo adzalowadi m'zipata za Yerusalemu.

13. Ndico cifukwa ca macimo a aneneri ndi mphulupulu za ansembeace,Amene anakhetsa mwazi wa olungama pakati pace.

14. Asocera m'makwalala ngati akhungu, aipsidwa ndi mwazi;Anthu sangakhudze zobvala zao.

15. Amapfuula kwa iwo, Cokani, osakonzeka inu, cokani, cokani, musakhudze kanthu.Pothawa iwo ndi kusocera, anthu anati mwa amitundu, Sadzagoneranso kuno.

16. Mkwiyo wa Yehova unawalekanitsa, sadzawasamaliranso;Iwo sanalemekeza ansembe, sanakomera mtima akulu.

17. Maso athu athedwa, tikali ndi moyo, poyembekeza thandizo cabe;Kudikira tinadikira mtundu wosatha kupulumutsa.

18. Amalondola mapazi athu, sitingayende m'makwalala athu;Citsiriziro cathu cayandikira, masiku athu akwaniridwa; pakuti citsiriziro cathu cafikadi.

19. Otilondola anaposa ziombankhanga za m'mlengalenga m'liwilo lao,Anatithamangitsa pamapiri natilalira m'cipululu.

20. Wodzozedwa wa Yehova, ndiye mpweya wa m'mphuno mwathu, anagwidwa m'maenje ao; Amene tinanena kuti, Tidzakhala m'mthunzi mwace pakati pa amitundu,

21. Kondwera nusangalale, mwana wamkazi wa Edomu, wokhala m'dzikola Uzi;Cikho cidzapita ngakhale mwa iwenso; udzaledzera ndi kubvulazako.

22. Mphulupulu yako yatha, mwana wamkazi wa Ziyoni, Yehova sadzakutenganso ndende;Koma adzazonda mphulupulu yako, mwana wa mkazi wa Edomu, nadzabvumbulutsa zocimwa zako.