15. Amapfuula kwa iwo, Cokani, osakonzeka inu, cokani, cokani, musakhudze kanthu.Pothawa iwo ndi kusocera, anthu anati mwa amitundu, Sadzagoneranso kuno.
16. Mkwiyo wa Yehova unawalekanitsa, sadzawasamaliranso;Iwo sanalemekeza ansembe, sanakomera mtima akulu.
17. Maso athu athedwa, tikali ndi moyo, poyembekeza thandizo cabe;Kudikira tinadikira mtundu wosatha kupulumutsa.
18. Amalondola mapazi athu, sitingayende m'makwalala athu;Citsiriziro cathu cayandikira, masiku athu akwaniridwa; pakuti citsiriziro cathu cafikadi.
19. Otilondola anaposa ziombankhanga za m'mlengalenga m'liwilo lao,Anatithamangitsa pamapiri natilalira m'cipululu.
20. Wodzozedwa wa Yehova, ndiye mpweya wa m'mphuno mwathu, anagwidwa m'maenje ao; Amene tinanena kuti, Tidzakhala m'mthunzi mwace pakati pa amitundu,
21. Kondwera nusangalale, mwana wamkazi wa Edomu, wokhala m'dzikola Uzi;Cikho cidzapita ngakhale mwa iwenso; udzaledzera ndi kubvulazako.
22. Mphulupulu yako yatha, mwana wamkazi wa Ziyoni, Yehova sadzakutenganso ndende;Koma adzazonda mphulupulu yako, mwana wa mkazi wa Edomu, nadzabvumbulutsa zocimwa zako.