20. Onani Yehova, nimupenye, mwacitira ayani ici?Kodi akazi adzadya zipatso zao, kunena ana amene anawaseweza?Kodi wansembe ndi mneneri adzaphedwa m'malo opatulika a Ambuye?
21. Wamng'ono ndi nkhalamba agona pansi m'makwalala;Anamwali ndi anyamata anga agwa ndi lupanga;Munawapha tsiku la mkwiyo wanu, munawagwaza osacitira cisoni.
22. Mwaitana zondiopsya mozungulira ngati tsiku la msonkhano;Panalibe wopulumuka ndi wotsala tsiku la mkwiyo wa Yehova;Omwe ndinawaseweza ndi kuwalera, adaniwo anawatsiriza.