Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 1:10-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Amaliwongo atambasulira manja ao pa zokondweretsa zace zonse;Pakuti waona amitundu atalowa m'malo ace opatulika,Amene munalamulira kuti asalowe mumsonkhano mwanu.

11. Anthu ace onse ausa moyo nafunafuna mkate;Ndi zokondweretsa zao agula zakudya kuti atsitsimutse moyo wao;Taonani, Yehova, nimupenye; pakuti ndasanduka wonyansa.

12. Kodi muyesa cimeneci cabe, nonsenu opita panjira?Penyani nimuone, kodi ciripo cisoni cina ngati cangaci amandimvetsa ine,Cimene Yehova wandisautsa naco tsiku la mkwiyo wace waukali?

13. Anatumiza moto wocokera kumwamba kulowa m'mafupa anga, unawagonjetsa;Wachera mapazi anga ukonde, wandibwezera m'mbuyo;Wandipululutsa ndi kundilefula tsiku lonse.

Werengani mutu wathunthu Maliro 1