Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Malaki 2:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo mudzadziwa kuti ndatumiza lamulo ili kwa inu, kuti cipangano canga cikhale ndi Levi, ati Yehova wa makamu.

5. Cipangano canga cinali naye ca moyo ndi ca mtendere; ndipo ndinampatsa izi kuti aope; nandiopa, naopsedwa cifukwa ca dzina langa.

6. Cilamulo ca zoona cinali m'kamwa mwace, ndi cosalungama sicinapezeka m'milomo mwace; anayenda nane mumtendere ndi moongoka, nabweza ambiri aleke mphulupulu,

7. Pakuti milomo ya wansembe iyenera kusunga cidziwitso, ndi anthu ayenera kufunafuna cilamulo pakamwa pace; pakuti iye ndiye mthenga wa Yehova wa makamu.

Werengani mutu wathunthu Malaki 2