Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Malaki 1:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Mwenzi atakhala wina mwa inu wakutseka pamakomo, kuti musasonkhe moto cabe pa guwa langa la nsembe! Sindikondwera nanu, ati Yehova wa makamu, ndipo sindidzalandira capereka m'dzanja lanu.

11. Pakuti kuyambira koturukira dzuwa kufikira kolowera kwace dzina langa lidzakhala lalikuru mwa amitundu; ndipo m'malo monse adzaperekera dzina langa cofukiza ndi copereka coona; pakuti dzina langa lidzakhala lalikuru mwa amitundu, ati Yehova wa makamu.

12. Koma inu muliipsa, pakunena inu, Gome la Yehova laipsidwa, ndi zipatso zace, cakudya cace, conyozeka.

Werengani mutu wathunthu Malaki 1