Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Malaki 1:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. KATUNDU wa mau a Yehova wa kwa Israyeli mwa Malaki.

2. Ndakukondani, ati Yehova; koma inu mukuti, Mwatikonda motani? Esau si mkulu wace wa Yakobo kodi? ati Yehova; ndipo ndinakonda Yakobo;

3. koma Esau ndinamuda, ndinasanduliza mapiri ace abwinja, ndi kupereka colowa cace kwa ankhandwe a m'cipululu.

4. Cinkana Edomu akuti, Taphwanyika, koma tidzabwera ndi kumanganso mabwinja; atero Yehova wa makamu, Adzamanga, koma Ine ndidzapasula; ndipo adzawacha, Dziko la coipa, ndiponso, Anthu amene Yehova akwiya nao cikwiyire.

Werengani mutu wathunthu Malaki 1