Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 9:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo Mose anati, Ici ndi cimene Yehova anakuuzani kuti mucicite; ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera kwa inu.

7. Ndipo Mose anati kwa Aroni, Sendera kufupi kwa guwa la nsembe, nukonze nsembe yako yaucimo, ndi nsembe yako yopsereza, nudzicitire wekha ndi anthuwo cotetetezera; nupereke coperekaca anthu, ndi kuwacitira cotetezera; monga Yehova anauza.

8. Pamenepo Aroni anasendera kufupi kwa guwa la nsembe, napha mwana wa ng'ombe wa nsembe yaucimo, ndiyo ya kwa iye yekha.

9. Ndipo ana a Aroni anasendera nao mwazi kwa iye; ndipo anabviika cala cace m'mwazimo naupaka pa nyanga za guwa la nsembe, nathira mwaziwo patsinde pa guwa la nsembe;

10. koma mafutawo, ndi imso, ndi cokuta ca mphafa za nsembe yaucimo, anazitentha pa guwa la nsembe; monga Yehova anauza Mose.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 9