Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 9:17-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo anabwera nayo nsembe yaufa, natengako wodzala dzanja, nautentha pa guwa la nsembe, angakhale adatentha nsembe yopsereza ya m'mawa.

18. Anaphanso ng'ombe, ndi nkhosa yamphongoyo, ndizo nsembe zoyamika za anthu; ndi ana a Aroni anapereka kwa iye mwaziwo, ndipo anauwaza pa guwa la nsembe pozungulira, ndi mafuta a ng'ombe;

19. ndi a nkhosa, ndi mcira wamafuta, ndi cophimba matumbo, ndi imso, ndi cokuta ca mphafa;

20. ndipo anaika mafuta pa ngangazo, natentha mafutawo pa guwa la nsembe.

21. Ndipo Aroni anaweyula ngangazo ndi mwendo wathako wa ku dzanja lamanja zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; monga iye anauza Mose.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 9