Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 9:12-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo anapha nsembe yopsereza; ndi ana a Aroni anapereka mwaziwo kwa iye, ndipo anauwaza pa guwa la nsembe pozu ngulira.

13. Ndipo anapereka nsembe yopsereza kwa iye, ciwalo ciwalo, ndi mutu wace; ndipo anazitentha pa guwa la nsembe.

14. Ndipo anatsuka matumbo ndi miyendo, nazitentha pa nsembe yopsereza pa guwa la nsembe.

15. Ndipo anabwera naco copereka ca anthu, natenga mbuzi ya nsembe yaucimo ndiyo ya kwa anthu, naipha, naipereka nsembe yaucimo, monga yoyamba ija.

16. Ndipo anabwera nayo nsembe yopsereza naipereka monga mwa lemba lace.

17. Ndipo anabwera nayo nsembe yaufa, natengako wodzala dzanja, nautentha pa guwa la nsembe, angakhale adatentha nsembe yopsereza ya m'mawa.

18. Anaphanso ng'ombe, ndi nkhosa yamphongoyo, ndizo nsembe zoyamika za anthu; ndi ana a Aroni anapereka kwa iye mwaziwo, ndipo anauwaza pa guwa la nsembe pozungulira, ndi mafuta a ng'ombe;

19. ndi a nkhosa, ndi mcira wamafuta, ndi cophimba matumbo, ndi imso, ndi cokuta ca mphafa;

20. ndipo anaika mafuta pa ngangazo, natentha mafutawo pa guwa la nsembe.

21. Ndipo Aroni anaweyula ngangazo ndi mwendo wathako wa ku dzanja lamanja zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; monga iye anauza Mose.

22. Ndipo Aroni anakweza dzanja lace kulozera anthu, nawadalitsa; natsika kuja anapereka nsembe yaucimo, ndi nsembe yopsereza, ndi nsembe zoyamika.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 9