Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 8:32-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Koma cotsalira ca nyama ndi mkate mucitenthe ndi moto.

33. Ndipo musaturuka pa khomo la cihema cokomanako masiku asanu ndi awiri, kufikira anakwanira masiku a kudzaza manja kwanu; pakuti adzaze manja anu masiku asanu ndi awiri.

34. Monga anacita lero lino, momwemo Yehova anauza kucita, kukucitirani cotetezera.

35. Ndipo mukhale pakhomo pa cihema cokomanako masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku, ndi kusunga cilangizo ca Yehova, kuti mungafe; pakuti anandiuza kotero.

36. Ndipo Aroni ndi ana ace amuna anacita zonse zimene Yehova anauza pa dzanja la Mose.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 8