Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 7:35-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. Ili ndi gawo la Aroni, ndi gawo la ana ace, locokera ku nsembe zamoto za Yehova, analinena, tsiku limene iye anawasendeza alowe utumiki wa ansembe a Yehova;

36. limene Yehova anauza ana a Israyeli aziwapatsa, tsiku limene iye anawadzoza. Likhale lemba losatha mwa mibadwo yao.

37. Ico ndi cilamulo ca nsembe yopsereza, ca nsembe yaufa, ca nsembe yaucimo, ndi ca nsembe yoparamula, ndi ca kudzaza dzanja, ndi ca nsembe zoyamika;

38. cimene Yehova analamulira Mose m'phiri la Sinai, tsikuli anauza ana a Israyeli abwere nazo zopereka zao kwa Yehova, m'cipululu ca Sinai.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 7