Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 7:21-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo munthu akakhudza cinthu codetsa, codetsa ca munthu, kapena codetsa ca zoweta, kapena ciri conse conyansa codetsa, nakadyako nyama ya nsembe zoyamika za Yehova, munthuyo asadzidwe kwa anthu a mtundu wace.

22. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

23. Lankhula ndi ana a Israyeli ndi kuti, Musamadya mafuta ali onse, a ng'ombe, kapena a nkhosa, kapena a mbuzi.

24. Ndipo mafuta a iyo idafa yokha, ndi mafuta a iyo idajiwa ndi cirombo ayenera nchito iri yonse, koma musamadya awa konse konse.

25. Pakuti ali yense akadya mafuta a nyama imene amabwera nayo ikhale nsembe yamoto ya kwa Yehova, munthu amene akadya awa asadzidwe kwa anthu a mtundu wace.

26. Ndipo musamadya mwazi uti wonse, kapena wa mbalame, kapena wa nyama, m'nyumba zanu zonse,

27. Ali yense akadya mwazi uti wonse, munthuyo asadzidwe kwa anthu a mtundu wace.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 7