Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 5:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. ndipo abwezere colakwira copatulikaco, naonjezepo limodzi la magawo asanu, napereke kwa wansembe; ndi wansembeyo amcitire comtetezera ndi nkhosa yamphongo ya nsembe yoparamula; ndipo adzakhululukidwa.

17. Ndipo munthu akacimwa, nakacita dna ca zinthu ziti zonse aziletsa Yehova; angakhale analibe kudziwa, koma waparamula, azisenza mphulupulu yace.

18. Nadze nayo kwa wansembe nkhosa yamphongo yopanda cirema ya m'khola lace, monga umayesa mtengo wace, ikhale nsembe yoparamula; ndipo wansembeyo amcitire comtetezera cifukwa ca kusacimwa dala kwace, osakudziwa; ndipo adzakhululukidwa.

19. Iyo ndiyo nsembe yoparamula; munthuyu anaparamula ndithu pamaso pa Yehova.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 5