Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 5:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo akacimwa munthu, wakuti adamva mau akuwalumbiritsa, ndiye mboni, kapena wakuona, kapena wakudziwa, koma osaulula, azisenza mphulupulu yace;

2. kapena munthu akakhudza ciri conse codetsa kapena mtembo wa nyama yodetsa, kapena mtembo wa coweta codetsa, kapena mtembo wa cokwawa codetsa, kungakhale kudambisikira, ali wodetsedwa, ndi woparamula.

3. Kapena akakhudza codetsa ca munthu, ndico codetsa ciri conse akakhala codetsedwa naco, ndipo cidambisikira; koma pocizindikira akhala woparamula:

4. kapena munthu akalumbira ndi milomo yace osalingirira kucita coipa, kapena kucita cabwino, ciri conse munthu akalumbira osalingirira, ndipo cidambisikira; koma pocizindikira akhala woparamula cimodzi ca izi:

5. ndipo kudzali, ataparamula cimodzi ca izi, aziulula cimene adacimwa naco;

6. nadze nayo nsembe yoparamula kwa Yehova cifukwa ca kulakwa kwace adacimwira, ndiyo msoti wa nkhosa, kapena msoti wa mbuzi, ukhale nsembe yaucimo; ndipo wansembe amcitire comtetezera cifukwa ca kucimwa kwace.

7. Ndipo cuma cace cikapanda kufikira nkhosa, wocimwayo adze nayo kwa Yehova nsembe yace yoparamula, njiwa ziwiri, kapena maunda awiri; imodzi ikhale ya nsembe yaucimo, ndi yina ya nsembe yopsereza.

8. Ndipo adze nazo kwa wansembe, ndiye ayambe kubwera nayo ija ya kwa nsembe yaucimo, napotole mutu wace pakhosi pace, osaucotsa;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 5