Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 4:33-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Naike dzanja lace pa mutu wa nsembe yaucimo, ndi kuipha ikhale nsembe yaucimo pamalo pophera nsembe yopsereza.

34. Ndipo wansembe atengeko mwazi wa nsembe yaucimo ndi cala cace, nauike pa nyanga za guwa la nsembe yopsereza, ndi kuthira mwazi wace wonse patsinde pa guwa la nsembe;

35. nawacotse mafuta ace onse, monga umo amacotsera mafuta a nkhosa pa nsembe yoyamika; ndipo wansembeyo atenthe, awa pa guwa la nsembe, monga umo amacitira nsembe zamoto za Yehova; ndipo wansembeyo amcitire comtetezera pa kucimwa kwace adakucimwira, ndipo adzakhululukidwa.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 4