Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 4:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Naturutse cikopa ca ng'ombeyo, ndi nyama yace yonse, pamodzi ndi mutu wace, ndi miyendo yace, ndi matumbo ace, ndi cipwidza cace,

12. inde ng'ombe yonse, kunja kwa cigono, kumka nayo kumalo koyera, kumene atayako mapulusa, naitenthe pankhuni ndi moto; aitenthe potayira mapulusa.

13. Ndipo khamu lonse la Israyeli likalakwa osati dala, ndipo cikabisika cinthuci pamaso pa msonkhano, litacita cina ca zinthu ziri zonse aziletsa Yehova, ndi kuparamula;

14. kukadziwika kucimwa adacimwako, pamenepo msonkhano uzibwera nayo ng'ombe yamphongo, ikhale nsembe yaucimo, ndipo udze nayo ku khomo la cihema cokomanako.

15. Ndipo akuru a khamulo aike manja ao pamutu pa ng'ombeyo, pamaso pa Yehova; naiphe ng'ombeyo pamaso pa Yehova.

16. Ndipo wansembe wodzozedwayo adze nao mwazi wina wa ng'ombeyo ku cihema cokomanako;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 4