Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 4:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2. Lankhula ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Munthu akacimwa, osati dala, pa cina ca zinthu ziri zonse aziletsa Mulungu, nakacitapo kanthu;

3. akalakwa wansembe wodzozedwa ndi kuparamulira anthu; pamenepo azibwera nayo kwa Yehova ng'ombe yamphongo, yopanda cirema, cifukwa ca kucimwa kwace adakucita, ikhale nsembe yaucimo.

4. Ndipo adze nayo ng'ombeyo ku khomo la cihema cokomanako pamaso pa Yehova; naike dzanja lace pamutu pa ng'ombeyo, naiphe ng'ombeyo pamaso pa Yehova.

5. Ndipo wansembe wodzozedwayo atengeko mwazi wa ng'ombeyo, nabwerenao ku cihema cokomanako;

6. ndipo wansembeyo abviike cala cace m'mwazimo, nawaze mwaziwo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova cakuno ca nsaru yocinga, ya malo opatulika.

7. Ndipo wansembeyo atengeko mwazi, nauike pa nyanga za guwa la nsembe la cofukiza ca pfungo lokoma, lokhala m'cihema cokomanako pamaso pa Yehova; nathire mwazi wonse wa ng'ombeyo patsinde pa guwa la nsembe yopsereza, lokhala pa khomo la cihema cokomanako.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 4