Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 3:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. naike dzanja lace pamutu pa copereka cace, naiphe patsogolo pa cihema cokomanako; ndipo ana a Aroni awaze mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.

9. Pamenepo abwere nayo nsembe yamoto ya kwa Yehova; yotengako ku nsembe yoyamika; mafuta ace, mcira wamafuta wonse, ataucotsa kufupi ku pfupa lao msana; naicotse mafuta akukuta matumbo, ndi mafuta onse akukhala pamatumbo,

10. ndi imso ziwiri, ndi mafuta ali pomwepo, okhala m'cuuno, ndi cokuta ca mphafa cofikira kuimso.

11. Ndipo wansembe azitenthe pa guwa la nsembe; ndico cakudya ca nsembe yamoto ya kwa Mulungu.

12. Ndipo copereka cace cikakhala mbuzi, azibwera nayo pamaso pa Yehova;

13. naike dzanja lace pamutu pace, naiphe pa khomo la cihema cokomanako; ndipo ana a Aroni awaze mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.

14. Ndipo abwere naco copereka cace cotengako, ndico nsembe yamoto ya kwa Yehova; acotse mafuta akukuta matumbo, ndi mafuta onse akukhala pamatumbo,

Werengani mutu wathunthu Levitiko 3