Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 27:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo iye wakuipatula akaombola nyumba yace, aonjezepo limodzi la magawo asanu la ndalama za kuyesa kwako, ndipo idzakhala yace.

16. Munthu akapatulirako Yehova munda wace wace, uziuyesa monga mwa mbeu zace zikakhala; homeri wa barie uuyese wa masekeli makumi asanu a siliva.

17. Akapatula munda wace kuyambira caka coliza lipenga, mundawo ukhale monga momwe unauyesera.

18. Akaupatula munda wace citapita caka coliza lipenga, wansembe azimwerengera ndalama monga mwa zaka zotsalira kufikira caka coliza lipenga, nazicepsako pa kuyesa kwako.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 27