Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 27:10-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Asaisinthe, yokoma m'malo mwa yoipa, kapena yoipa m'malo mwa yokoma; ndipo akasinthadi nyama m'malo mwa inzace, pamenepo iyo ndi yosinthikayo zikhale zopatulika.

11. Ndipo cikakhala ca nyama yodetsa, imene sabwera nayo ikhale copereka ca Yehova, aike nyamayi pamaso pa wansembe;

12. ndipo wansembeyo aiyese mtengo wace, ingakhale yokoma kapena yoipa; monga uiyesa wansembewe, momwemo.

13. Ndipo akaiombola ndithu, pamenepo aonjezepo limodzi la magawo asanu la mtengo wace.

14. Munthu akapatula nyumba yace ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe aziiyesa mtengo wace, ingakhale yokoma kapena yoipa; monga wansembeyo aiyesa, ikhale momwemo.

15. Ndipo iye wakuipatula akaombola nyumba yace, aonjezepo limodzi la magawo asanu la ndalama za kuyesa kwako, ndipo idzakhala yace.

16. Munthu akapatulirako Yehova munda wace wace, uziuyesa monga mwa mbeu zace zikakhala; homeri wa barie uuyese wa masekeli makumi asanu a siliva.

17. Akapatula munda wace kuyambira caka coliza lipenga, mundawo ukhale monga momwe unauyesera.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 27