Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 27:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Pamene munthu acita cowinda ca padera, anthuwo azikhala a Yehova monga mwa kuyesa kwako.

3. Ukayesa wamwamuna wa zaka makumi awiri kufikira wina wa zaka makumi asanu ndi limodzi, uziwayesera a masekeli makumi asanu a siliva, monga mwa sekeli wa malo opatulika.

4. Koma akakhala wamkazi, umuyesere wa masekeli makumi atatu.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 27