1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Pamene munthu acita cowinda ca padera, anthuwo azikhala a Yehova monga mwa kuyesa kwako.
3. Ukayesa wamwamuna wa zaka makumi awiri kufikira wina wa zaka makumi asanu ndi limodzi, uziwayesera a masekeli makumi asanu a siliva, monga mwa sekeli wa malo opatulika.
4. Koma akakhala wamkazi, umuyesere wa masekeli makumi atatu.