Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 26:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Asanu ainu adzapitikitsa zana limodzi, ndi zana limodzi la inu adzapitikitsa zikwi khumi; ndi adani anu adzagwa pamaso panu ndi lupanga.

9. Ndipo ndidzatembenukira kwa inu, ndi kukubalitsani, ndi kukucurukitsani; ndipo ndidzakhazika cipangano canga ndinapangana nanuco.

10. Ndipo mudzadya za sundwe wakale ndi kuturutsa zakale cifukwa ca zatsopano.

11. Ndidzamanga kacisi wanga pakati pa inu, ndipo moyo wanga sudzanyansidwa nanu.

12. Ndipo ndidzayendayenda pakati pa inu, ndi kukhala Mulungu wanu ndi inu mudzakhala anthu anga.

13. Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakuturutsani m'dziko la Aigupto, kuti musakhale akapolo ao; ndipo ndinatyola mitengo ya magoli anu, ndi kukuyendetsani coweramuka.

14. Koma mukapanda kundimvera Ine, osacita malamulo awa onse;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 26