Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 25:33-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Ndipo munthu akagula kwa Mlevi, nyumba yogulayo yokhala m'mudzi wace wace, ituruke m'caka coliza lipenga, popeza nyumba za m'midzi ya Alevi ndizo zao zao mwa ana a Israyeli.

34. Koma dambo la podyera pao siligulika; popeza ndilo lao lao kosatha.

35. Ndipo mbale wako akasaukira cuma, ndi dzanja lace lisowa; iwe uzimgwiriziza; akhale nawe monga mlendo wakugonera kwanu.

36. Usamambwezetsa phindu, kapena cioniezero; koma uope Mulungu wako; kuti mbale wako akhale nawe.

37. Musamampatsa ndarama zako polira phindu, kapena kumpatsa zakudya kuti aonjezerepo pocibwezera.

38. Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakuturutsani m'dziko la Aigupto, kukupatsani dziko la Kanani, kuti ndikhale Mulungu wanu.

39. Ndipo mbale wako akasaukira cuma, ndi kudzigulitsa kwa iwe; usamamgwiritsa nchito monga kapolo;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 25