Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 24:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Munthu akakantha munthu mnzace ali yense kuti afe, amuphe ndithu.

18. Munthu akakantha nyama kuti ife, ambwezere yina; moyo kulipa moyo.

19. Munthu akacititsa mnansi wace cirema, monga umo anacitira momwemo amcitire iye;

20. kutyola kulipa kutyola, diso kulipa diso, dzino kulipa dzino; monga umo anacitira munthu cirema, momwemo amcitire iye.

21. Iye wakukantha nyama kuti ife, ambwezere yina; iye wakupha munthu, amuphe.

22. Ciweruzo canu cifanefane ndi mlendo ndi wobadwa m'dziko; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 24