Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 23:25-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Musamagwira nchito ya masiku ena; mubwere nayo nsembe yamoto ya Yehova.

26. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

27. Komatu, tsiku lakhumi la mwezi uwu wacisanu ndi ciwiri, ndilo tsiku la citetezero; mukhale nao msonkhano wopatulika, ndipo mudzicepetse; ndi kubwera nayo nsembe yamoto kwa Yehova.

28. Musamagwira nchito iri yonse tsiku limenelo; pakuti ndilo tsiku la citetezero, kucita cotetezera inu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.

29. Pakuti munthu ali yense wosadzicepetsa tsiku limenelo, amsadze kwa anthu a mtundu wace.

30. Ndi munthu ali yense wakugwira nchito iri yonse tsiku limenelo, ndidzaononga munthuyo pakati pa anthu a mtundu wace.

31. Musamagwira nchito iri yonse; ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu, m'nyumba zanu zoo nse.

32. Likhale ndi inu Sabata lakupumula; ndipo mudzicepetse; tsiku lacisanu ndi cinai madzulo, kuyambira madzulo kufikira madzulo musunge Sabata lanu.

33. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

34. Nena ndi ana a Israyeli, kuti, Tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi uno wacisanu ndi ciwiri pali madyerero a misasa a Yehova, masiku asanu ndi awiri.

35. Tsiku loyamba likhale msonkhano wopatulika, musamagwira nchito ya masiku ena.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 23