Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 22:9-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Potero asunge cilangizo canga, angasenzepo ucimo, ndi kufera m'mwemo, pakuciipsa; Ine ndine Yehova wakuwapatula iwo,

10. Mlendo asadyeko copatulikaco; wakungokhala, ndi wansembe, kapena wolembedwa nchito, asadyeko copatulikaco.

11. Koma wansembe atakagula munthu ndi ndarama zace, iyeyu adyeko; ndi iwo amene anabadwa m'nyumba yace, adyeko mkate wace.

12. Ndipo mwana wamkazi wa wansembe akakwatibwa ndi mlendo, asadyeko nsembe yokweza ya zinthu zopatulika.

13. Koma mwana wamkazi wa wansembe akakhala wamasiye kapena wocotsedwa, ndipo alibe mwana, nabwerera ku nyumba ya atate wace, monga muja anali mwana, adyeko mkate wa atate wace; koma mlendo asamadyako.

14. Ndipo munthu akadyako cinthu copatulika mosadziwa, azionjezapo limodzi la magawo asanu, nalipereke kwa wansembe, pamodzi ndi copatulikaco.

15. Potero asaipse zinthu zopatulika za ana a Israyeli, zopereka iwo kwa Yehova;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 22