Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 22:20-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Musamabwera nayo yokhala ndi cirema; popeza siidzalandirikira inu.

21. Ndipo munthu akabwera nayo nsembe yoyamika kwa Yehova, ya pa cowinda cacikuru, kapena ya pa copereka caufulu, ya ng'ombe kapena nkhosa, ikhale yangwiro kuti ilandirike; ikhale yopanda cirema.

22. Musamabwera nazo kwa Yehova yakhungu, kapenayodukamwendokapena yopunduka, kapena yapfundo, kapena yausemwe, kapena ya usemwe waukuru, musamazipereka kwa Yehova nsembe zamoto pa guwa la nsembe.

23. Ng'ombe kapena nkhosa yokula kapena yocepa ciwalo, ikhale nsembe yaufulu; koma pa cowinda siidzalandirika.

24. Nyama yofula, kapena copwanya kapena cosansantha, kapena cotudzula, kapena codula, musamabwera nazo kwa Yehova; inde musamacicita ici m'dziko mwanu.

25. Ndipo musamazilandira izi ku dzanja la mlendo ndi kubwera nazo zikhale cakudya ca Mulungu wanu; popeza ziri nako kubvunda kwao; ziri ndi cirema; sizidzalandirikira inu.

26. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti, Zikamabadwa ng'ombe kapena nkhosa, kapena mbuzi, zikhale ndi mace masiku asanu ndi awiri;

27. kuyambira tsiku lacisanu ndi citatu ndi m'tsogolo mwace, idzalandirika ngati copereka nsembe yamoto ya Yehova.

28. Koma musamaipha ng'ombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wace tsiku limodzimodzi.

29. Ndipo mukamaphera Yehova nsembe yoyamika, muiphere kuti mulandirike.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 22