Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 22:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. kuti mulandiridwe, azibwera navo yaimuna yopanda cirema, ya ng'ombe, kapena nkhosa, kapena mbuzi.

20. Musamabwera nayo yokhala ndi cirema; popeza siidzalandirikira inu.

21. Ndipo munthu akabwera nayo nsembe yoyamika kwa Yehova, ya pa cowinda cacikuru, kapena ya pa copereka caufulu, ya ng'ombe kapena nkhosa, ikhale yangwiro kuti ilandirike; ikhale yopanda cirema.

22. Musamabwera nazo kwa Yehova yakhungu, kapenayodukamwendokapena yopunduka, kapena yapfundo, kapena yausemwe, kapena ya usemwe waukuru, musamazipereka kwa Yehova nsembe zamoto pa guwa la nsembe.

23. Ng'ombe kapena nkhosa yokula kapena yocepa ciwalo, ikhale nsembe yaufulu; koma pa cowinda siidzalandirika.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 22