Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 22:12-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo mwana wamkazi wa wansembe akakwatibwa ndi mlendo, asadyeko nsembe yokweza ya zinthu zopatulika.

13. Koma mwana wamkazi wa wansembe akakhala wamasiye kapena wocotsedwa, ndipo alibe mwana, nabwerera ku nyumba ya atate wace, monga muja anali mwana, adyeko mkate wa atate wace; koma mlendo asamadyako.

14. Ndipo munthu akadyako cinthu copatulika mosadziwa, azionjezapo limodzi la magawo asanu, nalipereke kwa wansembe, pamodzi ndi copatulikaco.

15. Potero asaipse zinthu zopatulika za ana a Israyeli, zopereka iwo kwa Yehova;

16. ndi kuwasenzetsa mphulupulu yakuwaparamulitsa, pakudya iwo zopatulika zao; pakuti Ine ndine Yehova wakuwapatula.

17. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

18. Nena ndi Aroni, ndi ana ace amuna, ndi ana onse a Israyeli, nuti nao, Ali yense wa mbumba ya Israyeli, kapena wa alendo ali m'Israyeli, akabwera naco copereka cace, monga mwa zowinda zao zonse, kapena monga mwa zopereka zaufulu zao, zimene abwera nazo kwa Yehova zikhale nsembe zopsereza;

19. kuti mulandiridwe, azibwera navo yaimuna yopanda cirema, ya ng'ombe, kapena nkhosa, kapena mbuzi.

20. Musamabwera nayo yokhala ndi cirema; popeza siidzalandirikira inu.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 22