Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 22:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo mwana wamkazi wa wansembe akakwatibwa ndi mlendo, asadyeko nsembe yokweza ya zinthu zopatulika.

13. Koma mwana wamkazi wa wansembe akakhala wamasiye kapena wocotsedwa, ndipo alibe mwana, nabwerera ku nyumba ya atate wace, monga muja anali mwana, adyeko mkate wa atate wace; koma mlendo asamadyako.

14. Ndipo munthu akadyako cinthu copatulika mosadziwa, azionjezapo limodzi la magawo asanu, nalipereke kwa wansembe, pamodzi ndi copatulikaco.

15. Potero asaipse zinthu zopatulika za ana a Israyeli, zopereka iwo kwa Yehova;

16. ndi kuwasenzetsa mphulupulu yakuwaparamulitsa, pakudya iwo zopatulika zao; pakuti Ine ndine Yehova wakuwapatula.

17. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

Werengani mutu wathunthu Levitiko 22