Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 21:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. kapena munthu wopunduka phazi kapena wopunduka dzanja,

20. kapena wowerama, kapena wamfupi msinkhu, kapena wopunduka diso, kapena munthu wamphere, kapena wacipere, kapena wopunduka kumoto.

21. Wa mbeu ya Aroni wansembe asayandikize mmodzi wokhala naco cirema, kupereka nsembe zamoto za Yehova; ali naco cirema asayandikize kupereka cakudya ca Mulungu wace.

22. Adye cakudya ca Mulungu wace, copatulikitsa, ndi copatulika;

23. koma asafike ku nsaru yocinga, asayandikize ku guwa la nsembe, popeza ali naco cirema; kuti angaipse malo anga opatulika; popeza Ine ndine Yehova wakuwapatula.

24. Momwemo Mose ananena ndi Aroni, ndi ana ace amuna, ndi ana onse a Israyeli.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 21