Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 20:6-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo munthu wakutembenukira kwa obwebweta ndi anyanga kuwatsata ndi cigololo, nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndipo ndidzamsadza kumcotsa pakati pa anthu a mtundu wace.

7. Cifukwa cace dzipatuleni, nimukhale oyera; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

8. Ndipo musunge malemba anga ndi kuwacita; Ine ndine Yehova wakupatula inu.

9. Pakuti ali yense wakutemberera atate wace kapena mai wace azimupha ndithu; watemberera atate wace kapena mai wace; mwazi wace ukhale pamutu pace.

10. Munthu akacita cigololo ndi mkazi wa mwini, popeza wacita cigololo ndi mkazi wa mnansi wace, awaphe nditho, mwamuna ndi mkazi onse awiri.

11. Munthu akagona naye mkazi wa atate wace, wabvula atate wace; awaphe ndithu onse awiri; mwazi wao ukhale pamtu pao.

12. Munthu akagona ndi mpongozi wace, awaphe onse awiri; acita cisokonezo; mwazi wao ukhale pamtu pao.

13. Munthu akagonana ndi mwamuna mnzace, monga amagonana ndi mkazi, acita conyansa onse awiri; awaphe ndithu; mwazi wao ukhale pamtu pao.

14. Munthu akatenga mkazi pamodzi ndi mai wace cocititsa manyazi ici; aziwatentha ndi moto, iye ndi iwowa; kuti pasakhale cocititsa manyazico pakati pa inu.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 20