Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 20:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. pamenepo nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndi banja lace, ndi kumsadza iye, ndi onse akumtsata ndi cigololo kukacita cigololo kwa Moleke, kuwacotsa pakati pa anthu a mtundu wao.

6. Ndipo munthu wakutembenukira kwa obwebweta ndi anyanga kuwatsata ndi cigololo, nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndipo ndidzamsadza kumcotsa pakati pa anthu a mtundu wace.

7. Cifukwa cace dzipatuleni, nimukhale oyera; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

8. Ndipo musunge malemba anga ndi kuwacita; Ine ndine Yehova wakupatula inu.

9. Pakuti ali yense wakutemberera atate wace kapena mai wace azimupha ndithu; watemberera atate wace kapena mai wace; mwazi wace ukhale pamutu pace.

10. Munthu akacita cigololo ndi mkazi wa mwini, popeza wacita cigololo ndi mkazi wa mnansi wace, awaphe nditho, mwamuna ndi mkazi onse awiri.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 20