Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 2:6-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Uphwanye, nuthirepo mafuta; ndiyo nsembe yaufa.

7. Ndipo copereka cako cikakhala nsembe yaufa ya mumphika, cikhale ca ufa wosalala ndi mafuta.

8. Ndipo ubwere nayo nsembe yaufa yopangika ndi izi kwa Yehova; ndipo atabwera naco kwa wansembe, iyeyo apite naco ku guwa la nsembe.

9. Ndipo wansembeyo atengeko cikumbutso pa nsembe yaufa, nacitenthe pa guwa la nsembe; ndico nsembe yamoto ya pfungo lokoma la kwa Yehova.

10. Ndipo cotsalira ca nsembe yaufa cikhale ca Aroni ndi ana ace; ndico copatulikitsa ca nsembe zamoto za Yehova.

11. Nsembe iri yonse yaufa, imene mubwera nayo kwa Yehova, isapangike ndi cotupitsa, pakuti musamatenthera Yehova nsembe yamoto yacotupitsa, kapena yauci.

12. Monga copereka ca zipatso zoyamba muzipereka izi: koma asazifukize pa guwa la nsembe zicite pfungo lokoma.

13. Ndipo copereka cako ciri conse ca nsembe yaufa uzicikoleretsa ndi mcere; usasowe mcere wa cipangano ca Mulungu wako pa nsembe yako yaufa; pa zopereka zako zonse uzipereka mcere.

14. Ndipo ukabwera nayo nsembe yaufa ya zipatso zoyamba kwa Yehova, uzibwera nayo nsembe yako ya zipatso zoyamba ikhale ya ngala zoyamba kuca, zoumika pamoto, zokonola.

15. Ndipo uthirepo mafuta, ndi kuikapo libona; ndiyo nsembe yaufa.

16. Ndipo wansembe atenthe cikumbutso cace, atatapa pa tirigu wace wokonola, ndi pa mafuta ace, ndi kutenga libano lace lonse; ndiyo nsembe yamoto ya kwa Yehova.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 2