Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 19:26-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Musamadya kanthu ndi mwazi wace; musamacita nyanga, kapena kuombeza ula.

27. Musamameta mduliro, kapena kusenga m'mphepete mwa ndebvu zanu,

28. Musamadziceka matupi anu cifukwa ca akufa, kapena kutema mpbini; Ine ndine Yehova.

29. Usamaipsa mwana wako wamkazi ndi kumcititsa cigololo; lingadzale ndi cigololo dzikoli, ndi kudzazidwa nazo zocititsa manyazi.

30. Muzisunga masabata anga, ndi kucitira ulemu malo anga opatulika; Ine ndine Yehova.

31. Musamatembenukira kwa obwebweta, kapena anyanga; musawafuna, ndi kudetsedwa nao; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

32. Pali aimvi uziwagwadira, nucitire ulemu munthu wokalamba; nuope Mulungu wako; lnendine Yehova.

33. Ndipo mlendo akagonera m'dziko mwanu, musamamsautsa.

34. Mlendo wakugonera kwa inu mumuyese pakati pa inu monga wa m'dziko momwemo; umkonde monga udzikonda wekha; popeza munali alendo m'dziko la Aigupto; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

35. Musamacita cisalungamo poweruza mlandu, poyesa utali wace, kulemera kwace, kapena kucuruka kwace.

36. Mukhale naco coyesera coona, miyeso yoona, era woona, bini woona; Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakuturutsani m'dziko la Aigupto.

37. Ndipo musamalire malemba anga onse, ndi maweruzo anga onse, ndi kuwacita; Ine ndine Yehova.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 19