26. Musamadya kanthu ndi mwazi wace; musamacita nyanga, kapena kuombeza ula.
27. Musamameta mduliro, kapena kusenga m'mphepete mwa ndebvu zanu,
28. Musamadziceka matupi anu cifukwa ca akufa, kapena kutema mpbini; Ine ndine Yehova.
29. Usamaipsa mwana wako wamkazi ndi kumcititsa cigololo; lingadzale ndi cigololo dzikoli, ndi kudzazidwa nazo zocititsa manyazi.
30. Muzisunga masabata anga, ndi kucitira ulemu malo anga opatulika; Ine ndine Yehova.
31. Musamatembenukira kwa obwebweta, kapena anyanga; musawafuna, ndi kudetsedwa nao; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
32. Pali aimvi uziwagwadira, nucitire ulemu munthu wokalamba; nuope Mulungu wako; lnendine Yehova.
33. Ndipo mlendo akagonera m'dziko mwanu, musamamsautsa.
34. Mlendo wakugonera kwa inu mumuyese pakati pa inu monga wa m'dziko momwemo; umkonde monga udzikonda wekha; popeza munali alendo m'dziko la Aigupto; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
35. Musamacita cisalungamo poweruza mlandu, poyesa utali wace, kulemera kwace, kapena kucuruka kwace.