Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 13:8-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. ndipo wansembe aone, ndipo taonani, ngati nkhanambo yapitirira khungu, wansembe amuche wodetsedwa, ndilo khate.

9. Pamene nthenda yakhate iri mwa munthu, azimfikitsa kwa wansembe;

10. ndipo wansembe aone, ndipo taonani, ngati pali cotupa coyera pakhungu, ndipo casanduliza tsitsi likhale loyera, ndipo pacotupa pali mnofu wofiira,

11. ndilo khate lakale pa khungu la thupi lace, ndipo wansembe amuche wodetsedwa; asambindikiritse popeza ali wodetsedwa.

12. Ndipo ngati khate libukabuka pakhungu, ndi khate lakuta khungu lonse la wanthendayo kuyambira mutu wace kufikira mapazi ace, monga momwe apenyera wansembe;

13. pamenepo wansembe aone, ndipo taonani, ngati khate lakuta thupi lace, amuche woyera wanthendayo; patuwa ponsepo; ndiye woyera.

14. Koma tsiku liri lonse ukaoneka pa iye mnofu wofiira, adzakhala wodetsedwa,

15. Ndipo wansembe aone mnofu wofiirawo, namuche wodetsedwa; mnofu wofiira ndiwo wodetsa; ndilo khate.

16. Kapena mnofu wofiira ukasandukanso, nusandulika wotuwa, afike kwa wansembe,

17. ndi wansembe amuone, ndipo taonani, ngati nthenda yasandulika yotuwa, wansembe amuche woyera wanthendayo; ndiye woyera.

18. Ndipo pamene thupi liri ndi cironda pakhungu pace, ndipo capola,

19. ndipo padali cironda pali cotupa coyera, kapena cikanga cotuuluka, pamenepo acionetse kwa wansembe; ndipo wansembe aone,

20. ndipo taonani, ngati cioneka cakumba kubzola khungu, ndipo tsitsi lace lisanduka lotuwa, pamenepo wansembe amuche wodetsedwa; ndiyo nthenda yakhate yabuka m'cirondamo.

21. Koma wansembe akaciona, ndipo taonani, palibe tsitsi loyera pamenepo, ndipo sicinakumba kubzola khungu, koma cazimba, pamenepo wansembe ambindikiritse masiku asanu ndi awiri;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 13