Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 13:54-58 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

54. pamenepo wansembe aziuza kuti atsuke cija pali khate, nacibindikiritse masiku asanu ndi awiri ena;

55. ndipo wansembe aone nthenda ataitsuka, ndipo taonani, ngati nthendayi siinasandulika maonekedwe ace, yosakulanso nthenda, ndico codetsedwa; ucitenthe ndi moto; ndilo pfunka, kungakhale kuyera kwace kuli patsogolo kapena kumbuyo.

56. Ndipo wansembe akaona, ndipo taonani, nthenda yazimba ataitsuka, pamenepo aikadzule pa cobvala, kapena cikopa, kapena muyaro, kapena mtsendero;

57. ndipo ikaonekabe pacobvala, ngakhale pamuyaro, kapena pamtsendero, kapena pa cinthu ciri conse copangika ndi cikopa, irikubukanso; ucitenthe ndi moto cija canthenda.

58. Ndipo ukatsuka cobvalaco, kapena muyaro, kapena mtsendero, kapena cinthu ciri conse copangika ndi cikopa, ngati nthenda yalekapo pa cimeneco, acitsukenso kawiri, pamenepo ciri coyera.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 13