Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 13:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Koma tsiku liri lonse ukaoneka pa iye mnofu wofiira, adzakhala wodetsedwa,

15. Ndipo wansembe aone mnofu wofiirawo, namuche wodetsedwa; mnofu wofiira ndiwo wodetsa; ndilo khate.

16. Kapena mnofu wofiira ukasandukanso, nusandulika wotuwa, afike kwa wansembe,

17. ndi wansembe amuone, ndipo taonani, ngati nthenda yasandulika yotuwa, wansembe amuche woyera wanthendayo; ndiye woyera.

18. Ndipo pamene thupi liri ndi cironda pakhungu pace, ndipo capola,

19. ndipo padali cironda pali cotupa coyera, kapena cikanga cotuuluka, pamenepo acionetse kwa wansembe; ndipo wansembe aone,

Werengani mutu wathunthu Levitiko 13