Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 10:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo ana a Aroni, Nadabu ndi Abihu anatenga yense mbale yace ya zofukiza, naikamo moto, naikapo cofukiza, nabwera nao pamaso pa Yehova moto wacilendo, umene sanawauza.

2. Ndipo panaturuka moto pamaso pa Yehova, nuwatha, nafa iwo pamaso pa Yehova.

3. Ndipo Mose anati kwa Aroni, Ici ndi cimene Yehova ananena, ndi kuti, Mwa iwo akundiyandikiza ndipatulidwa Ine, ndi pamaso pa anthu onse ndilemekezedwa. Ndipo Aroni anakhala cete.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 10